Yesu
ndi ndani?
Analoseredwa
ndi:
Daniel.
Ndinawona m’masompheya a usiku, taonani, anadza
ndi mitambo ya kumwamba wina ngati mwana wa munthu, nafika
kwa nkhalamba ya
kale lomwe; ndipo anamyandikizitsa pamaso pake. Ndipo
anampatsa ulamuliro, ndi
ulemelero, ndi ufumu, kuti anthu onse, ndi mitundu yonse
ya anthu, ndi manenedwe onse, amtumikire;
Ulamuliro wake ndi ulamuliro wosatha umene sudzachotsedwa,
ndi ufumu wake
sudzawonongeka. Daniel 7:13-14
Yesaya.
Pakuti kwa ife mwana wakhanda wababwa, Kwa ife
mwana
wamwamuna wapatsidwa; ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa
lake, ndipo
adzamutcha dzina lake Wodabwitsa,
Wauphungu, Mulungu wamphamvu, Atate wosatha, Kalonga
wamtendere. Za kuyenjezera
ulamuliro wake, ndi za mtendere sizidzatha pa mpando
wachifumu wa Davide, ndi
pa ufumu wake, kuwukhazikitsa, ndi kuwuchirikiza ndi
chiweruzo ndi chilungamo
kuyambira tsopano ndi kunkabe nthawi zosatha. Changu cha
Yehova wa makamu
chidzachita zimenezi. Yesaya 9:6-7
Ndipo zonsezi zinakhala kuti chikachitike
chonenedwa ndi Ambuye mwa mneneri, ndikuti "Onani namwali
adzaima,
Nadzabala mwana wamwamuna, ndipo adzamutcha dzina lake,
EMANUELI;
kuthandauuzira kwake, "MULUNGU NAFE."
Mateyu 1:22-23
Analambiridwa
ndi:
Anzeru a
kummawa.
Ndipo Iwo, m’mene anamva Kwa Mfumu ananyamuka;
ndipo onani, nyenyezi ija anayiwona kum’mawa inawatsogolera
Iwo, kufikira
inadza niima pamwamba pomwe panali kamwanako. Ndipo iwo
powona nyenyeziyo,
anakondwera ndichikondwelero chachikulu. Ndipo pofika
kunyumba anawona Mwanayo
ndi Maria amayi ake, ndipo anagwa pansi namgwadira iye;
namasula chuma chawo,
nampatsa iye mphatso, ndiye Golidi ndi Libano ndi
Mure. Mateyu 2:9-11
Ophunzira
ake.
Ndipo Pomwepo Yesu anatansa dzanja lake,
nam’gwira iye, nanena naye, iwe wokhulupilira pang’ono,
wakayikiranji mtima?
Ndipo pamene iwo analowa m’ngalawamo, mphepo inaleka. Ndipo
iwo amene anali
m’ngalawamo anamgwadira nanena
"Zoonadi, ndinu Mwana wa Mulungu." Mateyu 14:31-33
Ndipo ophunzira ake Khumi ndi m’modzi anamuka
ku Galileya, kuphiri kumene Yesu anawakonzera iwo. Ndipo
pamene anamuwona Iye,
anamlambira. Mateyu 28:16-17
Ndipo anatuluka nawo kufikira ku Betaniya;
nakweza manja Ake, nawadalitsa. Ndipo kunali, pakuwadalitsa
Iye analekana nawo,
natengedwa kunka kumwamba. Ndipo anamlambira Iye, nabwera ku
Yerusalemu ndi
chimwemwe chachikulu; ndipo anakhala chikhalire m’kachisi,
nayamika Mulungu.
Amen. Luka 24:50-53
Amai anamuona akumpachika pamtanda.
Ndipo iwo anachoka msanga kumanda,ndi mantha
ndikukondwera kwakukuru,nathamanga kukawuza ophunzira ake.
Ndipo onani, Yesu
anakomana nawo, nanena, Tikuwoneni. Ndipo iwo anadza,
namgwiraIye mapazi ake,
namgwadira. Pomwepo Yesu ananena kwa iwo “Musaope.” Mateyu
28:8-10
Wolemba
ndi:
Adani a
Yesu.
Koma Yesu anawayankha iwo, Atate wanga amagwira
ntchito kufikira tsopano, Inenso ndigwira ntchito. Chifukwa
cha ichi a Yuda
anawonjeza kufuna kumupha. Sichifukwa cha kuswa Sabata
kokha, komatu kuti
amadzichanso kuti Mulungu ndi Atate Ake; nadziyerekeza
wofanana ndi
Mulungu. Yohane 5:17-18
Ayuda anamyankha Iye, "Tili nalo lamulo
ife, ndipo monga mwalamulo ayenera kufa, chifukwa
anadziyerekeza kukhala Mwana
wa Mulungu." Yohane 19:7
Mtumwi Petulo.
Yesu anawafunsa yiwo. "Inu mumati kuti ine
ndine yani. Ndipo Simoni Petulo anayankha nati, "Inu ndinu
Khristu, Mwana
wa Mulungu wamoyo. Ndipo Yesu anamyankha iye nati, "Ndiwe
wodala, Simoni
Bar-Yona: pakuti thupi ndi mwazi sizinakuululire ichi, koma
Atate wanga
wakumwamba.” Mateyu 16:15-17
Mtumwi Tomasi.
Yesu anadza, makomo ali chitsekere, nayimilira
pakati pawo, nati, "Mtendere ukhale ndi Inu!" Pomwepo
ananena kwa Tomasi, "Bwera nacho
chala chako kuno, nuone manja anga; ndipo bwera nalo dzanja
lako, nuliike
kunthiti yanga, ndipo usakhale wosakhulupilira." Tomasi
anayankha nati kwa
Iye, "Ambuye wanga ndi Mulungu wanga!" Yesu ananena kwa iye,
"Chifukwa wandiona Ine, wakhulupilira: odala iwo
akukhulupilira angakhale
sanawone." Yohane 20:26-29
Yesu
Mwini.
Ndipo onse anati, "kodi ndinu Mwana wa
Mulungu?" Ndipo Iye anati Kwa Iwo, "Mwatero ndinu
amene." Luka 22:70
“Ine ndi Atate wanga ndife amodzi.” Yohane
10:30
“Iye amene waona Ine waonanso Atate Wanga.”
Yohane 14:9